1. Anthu omwe ali oyenela kupeleka Zakaat
2. Anthu omwe akuyenela kulandila Zakaat.
Monga tinafotokozera pa tanthauzo pa Zakaat lija (mutha kuona gawo loyambilira) zinaonetselatu kuti si munthu aliyense amene angapeleke zakaat ayi.
Zakaat ndi ibaadah, ndiye sangapange aliyense, komaso kuonjezera apo Zakaat ili ndi malamulo ake posiyanitsa ndi Swadaqah. Choncho monveka bwino titha kunena kuti:
Zakaat ndi yokakamizidwa kupereka kwa Msilamu, wammuna kaya wamkazi, mwana kaya wamkulu oti wafikila Nisaab komanso chuma chake chazungula chaka*
Mu ma qualities omwe takambawo tiyamba kuphwanya imodzi imodzi malingana ndi mmene Qur’an komaso ma Hadeeth akutiphunzitsira:
Msilamu
Monga takambira kuti Zakaat ndi ibaadah, kutanthauza kuti ndi mwambo wa Chipembedzo. Ndiye mwambo wa Chipembedzo cha Chisilamu samapanga munthu wamba koma Msilamu basi
Akapanga ibaadah munthu wamba asali Msilamu, ibaadahyo silandiridwa
Allah akuti
وَمَنْ أَرَادَ الْآخِرَةَ وَسَعَى لَهَا سَعْيَهَا وَهُوَ مُؤْمِنٌ فَأُولَئِكَ كَانَ سَعْيُهُم مَّشْكُورًا
Koma amene akufuna (kukalipidwa) moyo winawo nagwila ntchito yake (yoti akalioidweyo) uku ali okhulupilila, okhawo ndiomwe ntchito yawo ikathokozedwe (ikalipidwe) Surah Al-Isra, Verse 19
Moti tikafuna kugawa uthewa wa chisilamu kwa osakhulupilira tisawauze kuti apeleke zakaat kaye, koma tiwauze akhulupilire kaye kenako akakhulupilira kenako nkumazawauza za zakaat mu nthawi yake.
Wammuna kaya wankazi
Pankhani ya kapembedzedwe chisilamu sichimasiyanitsa pakati pa amuna ndi akazi kupatula zokhazo zomwe Allah ndi Mtumiki watiuza kuti izi apange awa okha
Allah akuti
وَمَن يَعْمَلْ مِنَ الصَّالِحَاتِ مِن ذَكَرٍ أَوْ أُنثَى وَهُوَ مُؤْمِنٌ فَأُولَئِكَ يَدْخُلُونَ الْجَنَّةَ وَلَا يُظْلَمُونَ نَقِيرًا
Ndipo yemwe ati agwile ntchito yabwino kaya wammuna kaya wankazi uku ali okhulupilila amenewa azalowa ku jannah ndipo sazapondelezedwa even pang’ono Surah An-Nisa, Verse 124
Pankhani yopereka specifically Allah ananena kuti
… والمتصدقين وَالْمُتَصَدِّقَاتِ…أَعَدَّ اللَّهُ لَهُم مَّغْفِرَةً وَأَجْرًا عَظِيمًا
… Opeleka chopeleka achimuna ndi achikazi… Allah wawakonzera chikhululuko ndi malipiro akulu Surah Al-Ahzab, Verse 35
Kupita ngati off-topic pang’ono anthu ena amaona ngati azimayi akuyenela kumapeleka zakaat.
Koma si choncho ayi nzimayi ayenela kupeleka Zakaat ngati akukwaniritsa zomwe tikambe apazi
Mtumiki anawauza azimayi kuti
يامعشر النساء تصدفن ، فإني رأيتكن أكثر أهل النار رواه البخاري
Inu azimayi! Muzipeleka chopeleka chifukwa ndinakuonani kuti ambili a inu akalowa ku moto
Mwana kaya wankulu
Ku Chisilamu ma ibaadah ambili amafunika kuti ochitayo akhale wamkulu okhwima nzeru, izi ndi monga swalah, kusala ndi zina. Koma Zakaat mwanaso amayenera apeleke. Mtumiki ananena kuti
ابتعوا بأموال اليتامى لا تأكلها الصدقة رواه الدارقطني وله شاهد في الموطى للمالك
Pangilani business chuma cha ana amisiye kuopela kuti chingathe kudyedwa ndi zakaat
Kuchokera mu Hadeeth imeneyi tikunva kuti ngakhale chuma cha mwana ndiye kuti payenela kuchotsedwapo ndalama ya zakaat ngati chili chofika mlingo. Nchifukwa chake Mtumiki akulangiza osunga chuma cha ana kuti azichipangila business. Otherwise akapanda kutero kuchotsa zakaat kutha kupungula kwambiri chumacho mpaka mwina kutha.
Nisaab
Nisaab (النصاب) ndi mlingo wachuma oti chuma chikafika pamenepo chiyambe kaperekedwa Zakaat.
Nisaab imasiyana malingana ndi mtundu wa chuma ndipo tikhala tikuona bwino za nisaab kutsogoloko in shaa Allah
Chuma chomwe sichinafike pa Nisaab zakaat sikuyenereka kuperekedwa. Mmalo mwake mwini wakeyo angopereka Swadaqah wamba basi
Kuzungulira chaka
Mtumiki anati
من استفاد مالاً فلا زكاة عليه حتى يحول علىه الحول عند ربه رواه الترمذي وصححه الألباني
Munthu amene wapeza chuma palibe kupereka Zakaat kwa iye mpaka chitazungulira chaka pamaso pa mbuye wake
Chaka pa nkhani ya Zakaat chimawerengedwa kudzera mu calendar ya chisilamu yoyendela mwezi yotha miyezi 12
Munthu akapeza chuma chokwanira Nisaab adikire mpaka chithe chaka kuchokera tsiku lomwe anachipezalo mpamene adzalamulidwe kupereka Zakaat. Koma ngati chaka sichinathe, palibe Zakaat.
Zimenezi ndizomwe zikuyenera kuti zikhalepo kuti Zakaat iperekedwe.
JAZAKALLAH BUT WE NEED MORE BAYAAN NOW DASYS U DONT SEND IT PLS